Article
President waku South Africa anazizimuka ndi video imene a Trump anaonesa pa mkumano wawo ku America

President waku South Africa anazizimuka ndi video imene a Trump anaonesa pa mkumano wawo ku America

Zinali za manyazi pamene President waku South Africa anazizimuka ndi video imene a Trump anaonesa ngati umboni pa mkumano wawo ku America.

President waku South Africa aCyril Ramaphosa anaitanidwa ndi a Donald Trump ku m'kumano umene unalipo ku White House kuti akakambilane pa zinthu zomwe zikuchitika ku South Africa ndikuona kuti America ingathandize po bwanji pa mavuto amene atakambilanewo.

M'kumanowu wachitika kusatila pamene a Trump anaitanisa azungu onse omwe amakhala ku South Africa kuti azipita ku America ngati ma refugees (only white Afrikaners). Chiganizo chi chinayambitsa debate mma social media pakuti ngakhale anthu aku America izi sizinawasangalase pakuti azungu aku South Africa wa anapasidwa chithandizo chokuti eni ma Americans ena akuzisowa.

Sopano izi zinanyanya pamene zinazadziwika kuti a Trump ananamizidwa kuti azungu aku South Africa wa akuzuzidwa ndiponso akuphedwa (genecide). Pakuti boma la South Africa linatsimikiza kuti nkhani yi nawo akuimva koyamba kuchokera ku America konko kuti dziko lawo likupha azungu, komanso a police aku South Africa ngakhale a UN anatinso nkhani yi sakuidziwa.

Ndiye pofuna kuti a Trump asaoneke kunama kapena kuchita manyazi kuti anapanga chiganizo kuchokera nkhani zongomva pa tweet iwowa anaitanisa mtsogoleri waku South Africa yu kuti akakambilane bwinobwino za nkhani yi komanso zina zotelo.

Ndiye posakhalisa a Trump anatulusa video imene imaonesa a Julius Malema amene ali wa mkulu wachipani cha (EFF). Ndipo mkulu yu ndiwotchuka ndikuyankhula mosabisa mawu, tsopano mu video imene anatulusa a Trump imaonesa mkuluyu akunena kuti "Azungu tilibe nanu ntchito, siyani minda imene muli nayoyo sikuti ingasowe osamala". Iwowa anapitiliza kunena kuti aonetsetsa kuti alande minda kwa azungu onse olo opanda chiloledzo cha president, mpaka ananena kuti "anthu aku South iphani azungu wa"

Moti zinali za manyazi president Ramaphosa kuonelera video imeneyi, koma iye anafotokoza kuti "South Africa ndi dziko la Democracy ndipo anthu amaloledwa kukamba zomwe afuna, koma si zikutanthauza kuti zomwe anena a Malema ndiye kuti iwo akugwilizana nazo chifukwa a Malema wo amaziyankhulira mbali yawo". President Ramaphosa anapitiliza kunenetsa kuti ma policy akunena a Malema si ma policy a boma ndipo izi iwo sangapange.

Koma Trump akuoneka kuti sizikumugwilabe mtima pakuti iyeyu Cholinga chake ndikuwaonesa anthu a dziko lake kuti sikuti analakwisa kuchita po kanthu za a Azungu aku South Africa. Ndipo kwa iyeyu apapa akuona kuti zatheka, chifukwa anachita kunena kuti a news mulembe zimenezi osati muzingolemba zonyoza zokha.

Inu Mukuona kuti kunali koyenela President Ramaphosa kukamumana ndi president Donald Trump ku white house yake ku America?

Admin Jeffrey

Comment Below

85 Comments

2025

2026

2025

2026

2025

2026

2025

2026

2025

Faithinah

Koma zomwe wapanga Trump zi it's funny🤣 koma ndichipongwe chachikulu

Dan banda

Asiyen kungoti Trump guys kukana khala kumalawi amene tikanakokelana basioapena kukavotaso

Raphael bright

Ine ndingofunako share yanga ndichokeko kumalawi ndipite ku Bukina faso am tiered with this country called Malawi

Anderson Kaphamtengo

He couldn't have gone there aaah shit

Ackim kasanga

At the end south Africa it will be like naughbour country we cannot fight with whites there more clever than us and there still running all African countries no matter what we got independence from

Abdullah sewero

Chifukwa Chan anthu akudafe azungu amatipezeler

Abdullah sewero

Chifukwa Chan anthu akudafe azungu amatipezeler

White Theba

Kodi wa ku Burkina Faso uja sangatiyendereko Ku Malawi kuno? Ndusungira maungu aku Mponela azawalawe

Sostano Mbewe Salira

Popeza atsogoleri amapembeza azungu aku America ndi Britain mpakedi anapitako. Koma sizoona kuti America izilowerera ma policy amaiko ena

Joseph Petro

Trump wapambanatu uyu ndiochenjera mix south African imalakhulutsa kwambili pa masamba achezo

Joseph Petro

Trump wapambanatu uyu ndiochenjera mix south African imalakhulutsa kwambili pa masamba achezo

Wiladi

Apopo samayenelaa cozz anthuwa samayankhulana bwwino pa Twitter what About ukumana live

Lex

Trump wagwilitsa ntchito mawu a otsutsa boma osati zoneza za boma. Had it been that it was said by the president himself or any minister from the gvt, linali vuto koma Trump wangokhala okula mtima. Mutu wakenso ndipo

Lephard chikuse

Yes he did well to meet with him.

Lizwelithini Blackskin

Chimene anawiniranso Ramaphosa sindikuchiwona, tufuna J. Malema ife

Hlarry

Yes, because he's aware of what Trump think and the cause from the beginning with evidence that can make him think of solving the issue

Vigo

Samayenera kupitako, we r Africans we can do whatever we want to!

Mbongizo

Ayi sikunali koyenera kukumana ndi Trump

John kapyola

Ayi wangotayapo chabe nthawi...africa is for africans...lets unite and make one africa

Unknown

Ramaphosa ndi kape

Memory Vyalema Kumwenda

Athana okha aona kuti atati....komano Trump anachita bwino mukuonesa kanemayo 🤣🤣🤣🤣

Wesley

Okay

Yamikan

A Trump ndiosokoneza

Kapalasa

🙌

Bryson stambuli

Athamangitsidwe kumene

Big man

Ramaphosa ndi kape

Elizabeth Tsoka

Zaulendo uno

Chancy Mkandawire

Yes ndi chifukwa chake adati kandimverere adakanena za mmaluwa. Kupanda kupitako Trump akadapitiliza kukhulupirira report la bodza. Kotero Ramamphosa wachita bwino kupita.

194

Za mdziko

Promise Kumwenda

Eya, Chifkwa choti Kupanga kukumana nawo ndi a Trump bwez akanakhulupiliradi kut ziko la south Africa likuzudzadi azungu, pomwe zili za bodza.

Andy J

akanati sanapite bwenzi Trump akuzimva kuopedwa

MCHAEL ROBERT

The thing is analakwitsa and we need to stand as one AFRICA through Traolie

Henry

💯💯

Petros MLACOOH Kasimba

Its high time for Africa to stand on its own.

Yami barbers

Shaaaa kmatu ndie kuli ma comment eeeh ine ndikufuna ndingolawa ai sanachite bwino kumupha😀

Jonathan Mkandawire

President Ramaphosa walakwitsadi kupita ku mkumanowo chifukwa ikhozaso kukhala big trap yomwe anakonza ma Americans chifukwa choti a Ramaphosawo ndi omwewoso amalinyoza dziko la America kuti even if America stops offering donations to them sikuti angasowe pogwira. A Ramaphosa akuyenera kusamala kwambiri coz azunguwo alinaye ntchito yaikulu yoti amulongosole

Emmanuel dzimbili

Yes pali zathu zina mulungu amalora kuti zithu zichitike cholinga zina ma plan ya munthu ilepheleke monga yemweyu Trump

Slaji

Sanalakwise chilichose chimatha ndi kukambirana

Kadzombe Richman

Akanati asapita Trump akanaona ngati Africa imamuopa apolo zakhala bwino

Kadawati

Yes kunali koyenera chifukwa panopa mayiko amu Africa chuma chavuta kodalira ndiku mayiko akulu akulu eg America nde amangoyenera kunama basi kupangira kuti zinthu ziwayendere aku South Africa

Praise Kasunda

Ndiye choptra ramaphosa kumnko ndichan osangomuuza Trump kut abwer ndi iyey wabwanj ngat amamufuna

Mushymalawi

Mmmh I don't have an idea

ESCOBAR DON

actually it was a bad idea kuchita except invitation ya stupid white Trump coz nyani ndi nyani oloko atasintha thengo..

Shaaaaa sosakhla zabwino

Shaaaaa zodakhala zabwino

Shaaaaa sosakhla zabwino

Shaaaaa zodakhala zabwino

Sam luhanga

Inde, chifukwa a ramaphosawo anapitirira kususa pa zimene akuchitira anthu a maiko ena including dziko lanthuli

Chipie vuka

Malema aponyapo ndemanga naye

Ras

Nkhani mukulemba ngati mukulembesa chatGPT🚮

William Chisale

Very gud of course, because trump accused south Africa because of video made by Malema(very wise guy) and now Ramamphosa made it clear so that Trump can make his mind 🙄

Shadreck

Kkkkkkk this is what we call phoney war when we comes to History hahahahaha infact Trump safuna zopusa

Abdullah Msosah

Malema waona awayankhanso 😂😂😂😂

Grace beib

Sizabwino zomwe wapanga Trump anakangokambira mwa bwinobwino

Blessings banda

Ku south Africa athu ake muthu alibe

Patrick chinthenga

I wish Trump could have eliminated

Abdul Rahim yassin

A lamaphosa samayenera kupita kukakumana ndi trump ayi koma trump ndamene amayenera kubwera Ku south Africa penapake azunguwa tisamangwavera chilichonse ayi akati mubwere kuli zokambirana ndbwino kuwauza kuti abwere iwowo chifukwa ndamene akufuna zokambirana mbuzi za Athu azungu

Vincent

Eeehe

Mphasoul

Trump naye angobwera ndi zilizonse akuisewelesa africa kwabasi

Chikwatulah Ferume

The pain truth that Trump should not invite ramaphosa all the way from Africa just to show him a video which was mounted by democracy people

Precious matinga

Zopeper

Robert Phiri

Azungu sometimes amangoona zomwe ife ali nazo vuto,but only tikamayakhula zoona koma ngati zili za chilungamo.

Samel kapito

Aaa stunt iy aa

Lamdmw

kunali koyela chifukwa panali zinthu xomwe ramaphosa amaganiza kt akuyenal kukambilana osati zomwe amaonazo komano trump sanalakwiseso kuika video chifukwa apopo amenyelaso ufulu anthu ena like makadi ndi mtundu wina wa anthu

Andrew mzamu

There was no problem in confronting the American president as long as he had told his cabinet that these things were said by anti-government groups.

Felix matope

Zokambilana zawo zinali zoenela coz chilungamo chaziwika, than kuti president olamula azizondedwa

Mary samangaya

Zovutat akachitatu masewela dziko lawoli lisauka

Happy Muhammed

Yaa ! It was gud that he went to the white house to found out wats going on about there Relationship..So if they a Problem in a relationship We need to settle down together 💟 In Which Trump is not But he loves South Africa, They want to combination so, I don't see anything wrong ..Just do wat is right.

Sanud kaluwa

I think zaenda momwe zinayenera kukhaliratu 👍😜

Chung boy Chigodola

Apapatu sanalakwise kukumanako akonze vutolo

Kelz Stng

Eyha ndpo znali zofunika kwambiri chifukwa apopo ramayo asintha znthu zna zkuchitika behind hm

Kachistar mw

Kunali kwabwino kuti akumane ankhonze mgwilizano

Samuel kanyinji

Ma president akwa Africa kukhulupirira kupempha vuto

upload your music with us to get maximum reach out!