Article
Anyamata awiri omwe anapha makolo awo pakufuna kulanda chuma, court likufuna kuwatulusa

Anyamata awiri omwe anapha makolo awo pakufuna kulanda chuma, court likufuna kuwatulusa

Anyamata awiri omwe anapha makolo awo ku California, court likuganiza zowakhululukila ndikuwatulusa.

Anyamata wa omwe dzina lawo ndi Erik & Lyle Menendez anamangidwa pa mulandu okupha mayi ndi bambo awo ku California Beverly Hills. Ndipo atapha makolo awowa anayesela kuti nkhani ayibise koma therapist wawo ndi amene anapangitsa kuti nkhani iwululike.

Sono zinayenda motele, Anyamata wa anagwilitsa ntchito mifuti kuti aphe makolo awowa ndipo anayesesa kuti zioneke ngati apanga izi ndi akuba chabe ndipo zinathekadi, koma patapita nthawi m'modzi mwaiwo anakamu fotokozera therapist wake kuti anapha makolo awo (paja anthu olemera ati amakafotokoza nkhawa zawo kwa therapist)

Tsopano therapist yo naye mtima posaugwila anakafotokozera ka chibwenzi kake, ndiye chibwenzi cho chitatha nkazi yo anakaulura nkhani yo ku police anyamata wo ndikunjatidwa kuti akakhale ku Ndende moyo wawo onse. Pa nthawi yo anyamata wo wina anali ali ndi Zaka 18, pomwe wina ali ndi Zaka 21.

Tsopano anyamata wa akhala ali ku Ndende tsopano kwa dzaka zothamangila 30, koma kwapezeka umboni okuti Iwowa anapha makolo awowa (makamaka bambo awo) chifukwa chokuti ankawachitila nkhaza komanso kuchita nawo za dama (sexual abuse) osati chifukwa chofuna kulanda chuma chokha ayi. Kotelo court lalengeza kuti koyenela kuti atuluke basi chifukwa akhala mundende zaka zambili kale.

Koma zitengela ngati board yoona za omwe akuyenela kutuluka dzaka zokhala mundende zisanakwane itsimikize. Kotelo alowa mu court kuti akamvetso nkhani yawo (parole hearing) koma lawyer wawo wapeleka chikhulupiliro kuti anthu wa atuluka. Nkhani yawo yi inachitika 1989 ndipo kunatuluka ma filimu komanso ma documentaries ambili okamba nkhani yi, ndiyotchuka ku America ko.

Chochitisa chidwi china m'chakuti ku court ko kunazaza azibale awo akwa bambo awo ndi malemu mayiwa wo kuti akufuna anthu wa atuluke, koma kuli ku Malawi kuno anthu otele achibale angaikileso kumboyo kuti atuluke?

Source : DAILY MAIL

Admin Jeffrey

Comment Below

55 Comments

Real

Kumalawi n'zosatheka?nanji Pali ndalama

T .chekani

Kumalawi ndie mzosatheka bro ......achibale ndiwomwe amayambitsa kut akangutuluka tikamutema kunyumba🀩

Kyton

Koma ngati achibalenso akuti atuluke ndiekuti mwina anabisa ndalama amenewo

Joseph Elad Chikaonda

Eeiissshh Ai ali ndi mwai ndithu mwinad atuluka pajah kwathu kuno ndimpaka ifah moyo wako onse mu ukalavula gaga wanyoo uku kurukuta mano mundende or patapedzeka umbon ngat umeneu😏😏😏

HB

Ndekuti makolo anawonjezadi😬

SECOND B TIMBA

atuluke fast ayamba kukalambatu

Ndaya

Ehhh

Gwebe manzy

Zachamba

Grace kaledzera

Afere komko

Arda Guler

Eish... Zovutatu

Warrior

Zofutatu

MWAI K BANDA

Kuli kuno ku Malawi πŸ‡²πŸ‡Ό si zingachitike kuti awabakile ayi nanji nanji Pali dollar po aaah ku πŸ‡²πŸ‡Ό eeeh amwene ndizina ZINATU kmso pena pake makolowo anafika posafika nawoso sibwino kuti anatibereka okha ndikutipangiraso nkhanza ayi kmsotu ma guy's woo ndekuti anafika potopa cfkwa anapanga zimenezo ingakhale kuti ndneyo singawaphe ayi km ndipita nawo ku police akakhala konko pomwe ndikafunile kukawatulusa akatuluka

Swaddle

Tiuzeni maina ama filimuwo tionere

Jaymore

They are still murderers

Enerst R chiphwafu

So sad kuli kumalawi sangakafikileso kumudzi kwao kuwausa akasake malo kwina

Alex de hero

Kkkkk mwamaliza ndi mwanosotu kkkk

Thengo thengo

Odya zake alibe mulandu my vote πŸ˜‚

Fuman Junior

Afana koma mwakalambatu

Bamboanyo

Zovutatu..koma atuluke

Chakwera my vote

Chakwera my vote

Chakwera

πŸ™ŒπŸ™Œine ndzavotera chakwera

Wake 808

Zovuta

Kwa ineyo akuyenela kutuluka Coz ndendeyo ayi nyoyisa kwa mbili mix so malem akuchimunawo amanjoyaasa kwa mafanawo yakumbuyo ,,waiona imeyo lowyer siwachibwana guys πŸ‘¦ 😜

Kwa ineyo akuyenela kutuluka coz ndendeyo ayi njoyisa kwa mbili mix so malem akuchimunawo so amanjoyaso kwa mafanawo yakumbuyo,,,,waiona imeneyo ,,lawyer siwachibwana guyz

Cactasnopal

Za anthu a chuma Ixi

Donald Trump

Lemme write in Chichewa "nkhaniyi ndiomvesa chisoni ndipo ine yandikhuza" πŸ₯ΊπŸ˜­

Yuzzy Yg Max

Nkhani za serious izi

Jackson

Yeah kumbali yanga akuyenela kutuluka ndithu zaka zachuluka zedi,komanso ngati mbali zonse ngati achibale aikila umboni kuti atuluke akuyenela kutuluka basi.

Ethel Mphonde

Timalakwisa ev day koma Mulungu amatikhululukira

Gift Lubani

Akuyeneradi kutulutsidwa

Peter Muthalika

Fotseki πŸ˜‚

Anderson Kaphamtengo

Let's wait for the parole hearing and I have the faith that these two guys are going to be free at last.

Bola

Bolatu

Bola

Bolatu

Dr Lazarus Chakwera

Anyamatawa aluyenera unjatidwa

Obvious frighton

Atuluke inu bodza 😹

Luka Thamanga

Kuli kumalawi kuno azifuna ndalama kuti atuluke

H~more

aaaa zawo izo πŸ˜‚πŸ’”

Milward Molson Tengatenga

Amawanyenga eti

Ellah

Sad

Maya

Zivuta

Jamie

Ooooh nde nkhan zake kodi😎

Binccoh

Zovutatu

Max-G

Bambo awo anali ankhanza anayeneraso kulandra nkhanza mxiii kuli kumalawi bwenz atamvekedwa teyala kale kale anawa

Tk

Koma bwezi atanena akuwapanga nkhazamo kae..bola chilungamo chadziwika...kuli kuno atawaika mu teyalaa sure

Daud B. Inussah

ku America nkhani zimayenda bwino not ku Malawi kuno

Vedai 248

OK!!!! πŸ˜…

Redd

Ndye mwat amawapakulaso?

Makosana

Zaziii A Jeffule

Fayson Emmanuel

Now mwayamba kubweletsa nkhani zabho

Mercy Zomba

Km ndiye zinangovuta kuti samakanena Kwa aliyese Maka pa khaza zomwe amkakumana nazo

Clifford Justin

It's some fing

Girro Misoya

Kwathu kuno sanatuluke ndipo sangakukhalire mboni athu akuno eeeπŸ˜…

Peter masi

Iiiiiiiih kom zina ukamva πŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™Œ

Vada Edw Mw

Zosayenda

Davie Mpombera

The justice system is still alive not here in malawi.

upload your music with us to get maximum reach out!